Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 27:9-15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndiyeno upange bwalo+ la chihema. Kumbali yakumʼmwera, bwalolo ulitchinge ndi mpanda wa nsalu za ulusi wopota wabwino kwambiri. Mpandawo ukhale mamita 45 mulitali mwake kumbali imodziyo.+ 10 Upangenso zipilala zake 20 ndi zitsulo 20 zakopa zokhazikapo zipilalazo. Tizitsulo ta zipilala tokolowekapo nsalu ndi tolumikizira take tikhale tasiliva. 11 Nsalu yambali yakumpoto kwa mpandawo ikhalenso mamita 45 mulitali mwake, ndipo kukhale zipilala 20 ndi zitsulo 20 zakopa zokhazikapo zipilalazo. Tizitsulo tokolowekapo nsalu ndi tolumikizira take tikhale tasiliva. 12 Mulifupi mwa bwalolo, kumbali yakumadzulo, mpanda wa nsaluwo kutalika kwake ukhale mamita 23, ndipo ukhale ndi zipilala 10 ndi zitsulo 10 zokhazikapo zipilalazo. 13 Ndipo mulifupi mwa bwalolo kumbali yakumʼmawa, kotulukira dzuwa, kukhale mamita 23. 14 Kudzanja lamanja la geti la bwalolo, mpanda wa nsaluwo ukhale mamita 7 kutalika kwake. Kukhale zipilala zitatu ndi zitsulo zitatu zokhazikapo zipilalazo.+ 15 Ndipo kudzanja lamanzere la geti la bwalolo mpanda wa nsaluwo ukhale mamita 7. Kukhale zipilala zitatu ndi zitsulo zitatu zokhazikapo zipilalazo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena