Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 25:35, 36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Mʼbale wanu akasauka pakati panu ndipo sangathe kudzisamalira, muzimuthandiza+ ngati mmene mungathandizire mlendo wokhala pakati panu,+ kuti nayenso akhale ndi moyo. 36 Musamalandire chiwongoladzanja kapena kupezerapo phindu+ pa iye.* Muziopa Mulungu wanu+ ndipo mʼbale wanu azikhala ndi moyo pakati panu.

  • Deuteronomo 23:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mʼbale wanu musamamulipiritse chiwongoladzanja pa ndalama,+ chakudya kapena pa chilichonse chimene munthu angafunepo chiwongoladzanja.

  • Luka 6:34, 35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Komanso, ngati mumakongoza popanda chiwongoladzanja kwa okhawo amene mukuyembekezera kuti adzabweza ngongoleyo, mudzapindula chiyani?+ Ochimwanso amakongoza ochimwa anzawo popanda chiwongoladzanja, kuti adzawabwezere zomwezo. 35 Mosiyana ndi zimenezo, inu pitirizani kukonda adani anu. Pitirizani kuchita zabwino ndi kukongoza popanda chiwongoladzanja, osayembekezera kulandira kalikonse.+ Mukatero, mphoto yanu idzakhala yaikulu ndipo mudzakhala ana a Wamʼmwambamwamba, chifukwa iye ndi wokoma mtima kwa osayamika ndi kwa oipa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena