13 Kenako amuna awiri opanda pake anabwera nʼkukhala kutsogolo kwa Naboti. Ndiyeno anayamba kupereka umboni wotsutsana ndi Naboti pamaso pa anthuwo. Iwo ananena kuti: “Naboti wanyoza Mulungu ndi mfumu!”+ Atatero anapita naye kunja kwa mzindawo nʼkukamuponya miyala mpaka kufa.+