10 Kwa zaka 6, muzidzala mbewu mʼminda yanu nʼkukolola mbewuzo.+ 11 Koma chaka cha 7 musamaulime, muziusiya kuti ugonere. Osauka amene ali pakati panu azidya zimene zili mʼmundamo ndipo zimene iwo asiya, nyama zakutchire zidzadya. Muzichita zimenezi ndi munda wanu wa mpesa komanso wa maolivi.