-
Luka 6:34, 35Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
34 Komanso, ngati mumakongoza popanda chiwongoladzanja kwa okhawo amene mukuyembekezera kuti adzabweza ngongoleyo, mudzapindula chiyani?+ Ochimwanso amakongoza ochimwa anzawo popanda chiwongoladzanja, kuti adzawabwezere zomwezo. 35 Mosiyana ndi zimenezo, inu pitirizani kukonda adani anu. Pitirizani kuchita zabwino ndi kukongoza popanda chiwongoladzanja, osayembekezera kulandira kalikonse.+ Mukatero, mphoto yanu idzakhala yaikulu ndipo mudzakhala ana a Wamʼmwambamwamba, chifukwa iye ndi wokoma mtima kwa osayamika ndi kwa oipa.+
-