Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 28:53
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 53 Zikadzatero mudzadya ana anu omwe,* mnofu wa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi+ amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, chifukwa cha mavuto oopsa amene mudzakumane nawo adani anu akadzakuzungulirani.

  • 2 Mafumu 6:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Choncho tinaphika mwana wanga nʼkumudya.+ Tsiku lotsatira ndinauza mayiyu kuti, ‘Bweretsa mwana wako timudye.’ Koma iye anakamʼbisa.”

  • Yeremiya 19:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Ndidzawachititsa kudya mnofu wa ana awo aamuna ndi ana awo aakazi. Aliyense adzadya mnzake chifukwa adani adzawazungulira komanso chifukwa chosowa mtengo wogwira. Izi zidzachitika pamene adani awo ndiponso anthu amene akufuna moyo wawo adzawapanikize.”’+

  • Maliro 4:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Azimayi amene amakhala achifundo, aphika ana awo ndi manja awo.+

      Anawo akhala chakudya chawo pa nthawi yachisoni pamene mwana wamkazi wa anthu anga wawonongedwa.+

  • Ezekieli 5:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Choncho azibambo amene ali mumzindawo adzadya ana awo+ ndipo ana adzadya abambo awo. Ine ndidzakulanga ndipo anthu ako onse otsala ndidzawabalalitsira kumbali zonse.”’+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena