53 Zikadzatero mudzadya ana anu omwe,* mnofu wa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi+ amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, chifukwa cha mavuto oopsa amene mudzakumane nawo adani anu akadzakuzungulirani.
10 Choncho azibambo amene ali mumzindawo adzadya ana awo+ ndipo ana adzadya abambo awo. Ine ndidzakulanga ndipo anthu ako onse otsala ndidzawabalalitsira kumbali zonse.”’+