Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 11:21-24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Pa tizilombo tonse timene timapezeka tambiri, tamapiko ndiponso timayenda ndi miyendo yonse 4, mungathe kudya tizilombo tokhato timene tili ndi miyendo iwiri italiitali yolumphira. 22 Tizilombo timene mungadye ndi iti: mitundu yosiyanasiyana ya dzombe loyenda mitunda italiitali, mitundu ina ya dzombe lodyedwa,+ nkhululu ndi ziwala. 23 Koma tizilombo tina tonse timene timapezeka tambiri, tamapiko ndiponso tamiyendo 4, ndi tonyansa kwa inu. 24 Zamoyo zimenezi nʼzimene mungadzidetse nazo. Aliyense wokhudza zamoyo zimenezi zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.+

  • Levitiko 17:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ngati munthu aliyense wadya nyama imene waipeza yakufa kapena imene yaphedwa ndi chilombo,+ kaya akhale nzika kapena mlendo wokhala pakati panu, munthu ameneyo azichapa zovala zake nʼkusamba thupi lonse, ndipo azikhala wodetsedwa mpaka madzulo.+ Kenako azikhala woyera.

  • Deuteronomo 14:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Musamadyenso nkhumba chifukwa ndi ya ziboda zogawanika koma sibzikula. Imeneyi ndi yodetsedwa kwa inu. Musamadye nyama yake kapena kuikhudza ikafa.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena