Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 18:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Mose anasankha amuna oyenerera mu Isiraeli monse kuti akhale atsogoleri a anthu. Anasankha atsogoleri a magulu a anthu 1,000, atsogoleri a magulu a anthu 100, atsogoleri a magulu a anthu 50 ndi atsogoleri a magulu a anthu 10.

  • Numeri 1:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Amenewa ndi amene anasankhidwa pa gulu la anthuwo. Iwo anali atsogoleri+ a mafuko a makolo awo, atsogoleri a anthu masauzande mu Isiraeli.”+

  • Yoswa 22:13, 14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Kenako Aisiraeli anatumiza Pinihasi+ mwana wa wansembe Eleazara, kwa anthu a fuko la Rubeni, la Gadi ndi hafu ya fuko la Manase, ku Giliyadi. 14 Anamʼtumiza pamodzi ndi atsogoleri 10. Fuko lililonse la Isiraeli linatumiza mtsogoleri mmodzi woimira nyumba ya makolo ake. Mtsogoleri aliyense anali woimira nyumba ya bambo ake pakati pa Aisiraeli masauzande.+

  • Yoswa 23:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Yoswa anaitana Aisiraeli onse,+ akulu awo, atsogoleri, oweruza ndi akapitawo+ nʼkuwauza kuti: “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.

  • 1 Mbiri 27:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Awa ndi magulu a Aisiraeli amene anali atsogoleri a nyumba za makolo awo, atsogoleri a magulu a anthu 1,000, atsogoleri a magulu a anthu 100+ ndiponso anthu omwe ankatumikira mfumu+ pa nkhani iliyonse yokhudza magulu amenewa. Maguluwa ankasinthanasinthana mwezi uliwonse pa chaka ndipo gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena