Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 17:5, 6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Kenako Yehova anauza Mose kuti: “Tsogola ndipo utenge ena mwa akulu a Isiraeli komanso ndodo yako imene unamenya nayo mtsinje wa Nailo.+ Uitenge mʼdzanja lako ndipo uziyenda. 6 Tamvera! Ine ndidzatsogola nʼkukaima pathanthwe ku Horebe. Kumeneko ukamenye thanthwelo ndipo padzatuluka madzi amene anthu adzamwe.”+ Mose anachitadi zomwezo pamaso pa akulu a Isiraeli.

  • Salimo 78:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu,

      Anawalola kumwa madziwo mpaka ludzu kutha ngati kuti akumwa madzi amʼnyanja.+

  • Salimo 105:41
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 41 Anatsegula thanthwe ndipo panatuluka madzi ambiri.+

      Madziwo anayenda ngati mtsinje kudutsa mʼchipululu.+

  • Salimo 114:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 Amene amasintha thanthwe kukhala dambo la madzi,

      Komanso mwala wa nsangalabwi kukhala akasupe a madzi.+

  • Yesaya 48:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Iwo sanamve ludzu pamene iye ankawatsogolera kudutsa mʼchipululu.+

      Iye anachititsa kuti madzi atuluke pathanthwe kuti iwo amwe.

      Anangʼamba thanthwe nʼkupangitsa kuti madzi atuluke.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena