Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 9:23, 24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Pamapeto pake Mose ndi Aroni analowa mʼchihema chokumanako, kenako anatulukamo nʼkudalitsa anthuwo.+

      Atatero ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse,+ 24 ndipo moto unatsika kuchokera kwa Yehova+ nʼkunyeketsa nsembe yopsereza ndiponso mafuta, zimene zinali paguwa lansembe. Anthu onse ataona zimenezi anayamba kufuula mokondwera ndipo anagwada nʼkuwerama mpaka nkhope zawo pansi.+

  • Deuteronomo 4:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Chifukwa Yehova Mulungu wanu ndi moto wowononga,+ iye ndi Mulungu amene amafuna kuti anthu azidzipereka kwa iye yekha basi.+

  • Oweruza 6:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Kenako mngelo wa Yehova anakhudza nyama ndi mikateyo ndi nsonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake. Atatero, moto unayaka pamwalawo nʼkuwotcheratu nyama ndi mkatewo.+ Zitatero mngelo wa Yehovayo anazimiririka.

  • 1 Mbiri 21:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Ndiyeno Davide anamangira Yehova guwa lansembe+ pamalowo ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zamgwirizano. Komanso anaitana pa dzina la Yehova ndipo tsopano anamuyankha potumiza moto+ kuchokera kumwamba umene unafika paguwa lansembe yopsereza.

  • 2 Mbiri 7:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Solomo atangomaliza kupemphera,+ moto unatsika kuchokera kumwamba+ nʼkutentha nsembe yopsereza ndiponso nsembe zina ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza nyumbayo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena