Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 45:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere.

      Mubwere pamodzi, inu anthu amene mwapulumuka ku mitundu ya anthu.+

      Amene amanyamula zifaniziro zawo zogoba sadziwa chilichonse

      Ndipo amapemphera kwa mulungu woti sangawapulumutse.+

  • Yeremiya 10:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  5 Mafanowo ali ngati choopsezera mbalame mʼmunda wa minkhaka ndipo sangalankhule.+

      Iwo amafunika kunyamulidwa chifukwa sangayende okha.+

      Musamachite mantha ndi mafano chifukwa sangakuvulazeni,

      Komanso sangachite chilichonse chabwino.”+

  • Danieli 5:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Mʼmalomwake mwadzikweza pamaso pa Ambuye wakumwamba+ ndipo munalamula anthu kuti akubweretsereni ziwiya zamʼnyumba yake.+ Ndiyeno inuyo, nduna zanu, adzakazi anu ndi akazi anu ena mwamwera vinyo mʼziwiya zimenezi ndipo mwatamanda milungu yasiliva, yagolide, yakopa, yachitsulo, yamitengo ndi yamiyala imene siona, kumva kapena kudziwa chilichonse.+ Koma Mulungu amene amakupatsani mpweya komanso amene ali ndi mphamvu zolamulira moyo wanu, simunamulemekeze.+

  • Habakuku 2:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Kodi chifaniziro chosema chili ndi phindu lanji,

      Pamene munthu wachisema?

      Nanga chifaniziro chachitsulo ndi mphunzitsi wonama zili ndi phindu lanji,

      Ngakhale kuti wochipanga amachikhulupirira,

      Nʼkumapanga milungu yopanda pake yosalankhula?+

      19 Tsoka kwa munthu amene amauza chikuni kuti: “Dzuka!”

      Kapena mwala wosalankhula kuti: “Dzuka! Tipatse malangizo”!

      Taona! Fanolo lakutidwa ndi golide ndi siliva,+

      Ndipo mkati mwake mulibe mpweya.+

  • 1 Akorinto 8:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ndiyeno pa nkhani ya kudya zakudya zoperekedwa kwa mafano, timadziwa kuti fano si kanthu+ ndiponso kuti kulibe Mulungu wina koma mmodzi yekha.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena