-
Yesaya 44:19, 20Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Palibe amene amaganiza mumtima mwake
Kapena amene akudziwa zinthu, kapenanso amene amamvetsa zinthu kuti adzifunse kuti:
“Hafu ya mtengowu ndasonkhera moto,
Ndipo pamakala ake ndaphikapo mkate komanso ndawotcha nyama nʼkudya.
Ndiye kodi wotsalawu ndipangire chinthu chonyansa?+
Kodi zoona ndilambire chinthu chopangidwa ndi mtengo?”*
20 Iye akudya phulusa.
Mtima wake umene wapusitsidwa wamusocheretsa.
Iye sangathe kudzipulumutsa kapena kunena kuti:
“Kodi chinthu chimene chili mʼdzanja langa lamanjachi si chabodza?”
-