Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 29:24, 25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 ana anu ndi alendo komanso mitundu yonse adzanena kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachitira dzikoli zimenezi?+ Nʼchiyani chachititsa kuti mkwiyo wake uyake kwambiri chonchi?’ 25 Ndiyeno iwo adzanena kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti anaphwanya pangano la Yehova,+ Mulungu wa makolo awo, limene anapangana nawo pamene ankawatulutsa mʼdziko la Iguputo.+

  • Oweruza 2:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Pamapeto pake, Yehova anakwiyira kwambiri Aisiraeli+ ndipo anati: “Popeza mtundu umenewu waphwanya pangano langa+ limene ndinalamula makolo awo kuti alisunge, ndipo sanandimvere,+

  • 1 Mafumu 8:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Mu Likasalo munalibe chinthu china chilichonse kupatulapo miyala iwiri yosema+ imene Mose anaikamo+ ku Horebe. Anaiikamo pa nthawi imene Yehova anachita pangano+ ndi Aisiraeli, pamene ankachoka mʼdziko la Iguputo.+

  • 2 Mafumu 17:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Iwo anapitiriza kukana malamulo ndi pangano+ limene iye anachita ndi makolo awo, ndiponso zikumbutso zimene iye anawapatsa powachenjeza.+ Mʼmalomwake ankatsatira mafano opanda pake+ ndipo nawonso anakhala opanda pake.+ Ankatengera mitundu yowazungulira imene Yehova anawalamula kuti asamaitsanzire.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena