Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 9:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndiyeno Yehu+ mwana wa Yehosafati mwana wa Nimusi, anakonzera Yehoramu chiwembu.

      Yehoramu ankalondera Ramoti-giliyadi+ pamodzi ndi Aisiraeli onse, chifukwa cha Hazaeli+ mfumu ya Siriya.

  • 2 Mafumu 9:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Zitatero Yehu anakoka uta wake nʼkubaya Yehoramu kumsana pakati pamapewa mpaka muviwo unatulukira pamtima pake ndipo Yehoramu anagwa mʼgaleta lake lankhondo.

  • 2 Mafumu 10:6, 7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Kenako Yehu anawalemberanso kalata ina yonena kuti: “Ngati muli kumbali yanga ndipo muzimvera mawu anga, mudule mitu ya ana aamuna a mbuye wanu ndipo mawa nthawi ngati yomwe ino mubwere nayo ku Yezereeli kuno.”

      Ana 70 a mfumuwo ankakhala ndi akuluakulu a mumzindawo omwe ankawasamalira. 7 Anthuwo atangolandira kalatayo, anatenga ana a mfumu 70 aja nʼkuwapha.+ Kenako anatenga mitu yawo nʼkuiika mʼmadengu ndipo anaitumiza kwa Yehu ku Yezereeli.

  • 2 Mafumu 10:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Kenako Yehu ndi Yehonadabu+ mwana wa Rekabu analowa mʼkachisimo. Ndiyeno Yehu anauza anthu olambira Baala kuti: “Fufuzani mosamala ndipo muonetsetse kuti muno mulibe aliyense wolambira Yehova, koma olambira Baala okhaokha.”

  • 2 Mafumu 10:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Yehu atangomaliza kupereka nsembe yopserezayo, anauza asilikali ake othamanga ndi othandiza pamagaleta kuti: “Lowani muwaphe! Pasapezeke aliyense wothawira panja.”+ Choncho asilikali othamanga ndi othandiza pamagaletawo anayamba kupha anthuwo ndi lupanga nʼkumaponya mitembo yawo panja. Anakafika mpaka mʼchipinda chamkati* cha kachisi wa Baalayo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena