Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 12:4, 5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Yehoasi anauza ansembe kuti: “Mutenge ndalama zonse zimene anthu akubweretsa kunyumba ya Yehova za zopereka zopatulika,+ zomwe ndi ndalama za msonkho zimene munthu aliyense akupereka,+ ndalama zoperekedwa ndi anthu amene analonjeza ndiponso ndalama zonse zimene munthu aliyense watsimikiza mumtima mwake kuti abweretse kunyumba ya Yehova.+ 5 Wansembe aliyense azitenga ndalama zimenezi kwa anthu omwe apereka nʼkuzigwiritsa ntchito kukonza paliponse pamene nyumbayi yawonongeka.”*+

  • 2 Mbiri 29:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Hezekiya+ anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 29. Mayi ake dzina lawo linali Abiya mwana wa Zekariya.+

  • 2 Mbiri 29:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Mʼchaka choyamba cha ulamuliro wake, mʼmwezi woyamba, iye anatsegula zitseko za nyumba ya Yehova komanso anazikonza.+

  • 2 Mbiri 34:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iwo anapita kwa Hilikiya mkulu wa ansembe nʼkumupatsa ndalama zimene anthu ankabweretsa kunyumba ya Mulungu, zimene Alevi omwe anali alonda apakhomo, anatolera kwa anthu a fuko la Manase, la Efuraimu, kwa Aisiraeli onse,+ kwa Ayuda onse, anthu a fuko la Benjamini ndiponso kwa anthu onse okhala ku Yerusalemu. 10 Kenako ndalamazo anazipereka kwa anthu amene anasankhidwa kuti aziyangʼanira ntchito panyumba ya Yehova. Ndiyeno anthu amene ankagwira ntchito panyumba ya Yehova anagwiritsa ntchito ndalamazo pokonza nyumbayo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena