Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ezara 5:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Komanso, mfumu Koresi inachotsa mʼkachisi wa ku Babulo ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara anazitenga mʼkachisi wa Mulungu yemwe anali ku Yerusalemu, nʼkupita nazo kukachisi wa ku Babuloyo.+ Ndiyeno anazipereka kwa munthu wina dzina lake Sezibazara,*+ amene Koresi anamusankha kuti akhale bwanamkubwa.+

  • Ezara 5:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Sezibazarayo atabwera anamanga maziko a nyumba ya Mulungu+ yomwe ili ku Yerusalemu. Kuyambira nthawi imeneyo mpaka pano nyumbayi ikumangidwabe ndipo sinamalizidwe.’+

  • Hagai 1:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 1 Mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Mfumu Dariyo, mʼmwezi wa 6, pa tsiku loyamba la mweziwo, mawu a Yehova anafika kwa Zerubabele+ yemwe anali bwanamkubwa wa Yuda mwana wa Salatiyeli, ndiponso kwa Yoswa yemwe anali mkulu wa ansembe mwana wa Yehozadaki. Mawuwa anafika kwa anthu amenewa kudzera mwa mneneri Hagai*+ kuti:

  • Hagai 1:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Choncho Yehova analimbikitsa+ Zerubabele mwana wa Salatiyeli bwanamkubwa wa Yuda,+ Yoswa+ mwana wa Yehozadaki mkulu wa ansembe ndiponso anthu ena onse. Ndipo iwo anabwera nʼkuyamba kugwira ntchito panyumba ya Mulungu wawo, Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+

  • Hagai 2:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti, ‘Pa tsiku limenelo ndidzakutenga iwe Zerubabele+ mwana wa Salatiyeli,+ mtumiki wanga,’ watero Yehova. ‘Ndipo ndidzachititsa kuti ukhale ngati mphete yodindira chifukwa iwe ndi amene ndakusankha,’ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena