-
Ezara 4:1-3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Adani a Yuda ndi Benjamini+ atamva kuti anthu amene anabwera kuchokera ku ukapolo+ akumangira kachisi Yehova Mulungu wa Isiraeli, 2 nthawi yomweyo anapita kwa Zerubabele ndi atsogoleri a nyumba za makolo nʼkukawauza kuti: “Bwanji tizimanga limodzi chifukwa ifeyo, mofanana ndi inuyo, timalambira* Mulungu wanu.+ Komanso timapereka nsembe kwa iye kuyambira mʼmasiku a Esari-hadoni+ mfumu ya Asuri, yemwe anatibweretsa kuno.”+ 3 Koma Zerubabele, Yesuwa ndi atsogoleri ena onse a nyumba za makolo za Isiraeli anawayankha kuti: “Sizingatheke kuti timange nyumba ya Mulungu wathu limodzi ndi inu.+ Timanga tokha nyumba ya Yehova Mulungu wa Isiraeli, mogwirizana ndi zimene Mfumu Koresi ya Perisiya yatilamula.”+
-