2 Muzikumbukira njira yaitali imene Yehova Mulungu wanu anakuyendetsani mʼchipululu zaka 40 zonsezi.+ Iye anakuyendetsani mʼchipululu kuti akuphunzitseni kudzichepetsa komanso kukuyesani+ pofuna kudziwa zimene zinali mumtima mwanu,+ kuti aone ngati mungasunge malamulo ake kapena ayi.