Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 4:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Koma samalani ndipo mukhale tcheru* kuti musaiwale zinthu zimene maso anu anaona, komanso kuti zinthu zimenezo zisachoke mumtima mwanu masiku onse a moyo wanu. Ana anu ndi zidzukulu zanu muziwauzanso zinthu zimenezo.+

  • Deuteronomo 6:6, 7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Mawu awa amene ndikukulamulani lerowa azikhala pamtima panu, 7 ndipo muziwakhomereza* mumtima mwa ana anu.+ Muzilankhula nawo mawuwo mukakhala pansi mʼnyumba mwanu, mukamayenda pamsewu, mukamagona komanso mukadzuka.+

  • Deuteronomo 6:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 mwana wanuyo mudzamuyankhe kuti, ‘Tinali akapolo a Farao ku Iguputo, koma Yehova anatitulutsa ku Iguputoko ndi dzanja lamphamvu.

  • Deuteronomo 11:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Mawu angawa muwasunge mʼmitima yanu ndipo muziwatsatira pa moyo wanu. Muwamange padzanja lanu kuti muziwakumbukira ndipo akhale ngati chomanga pachipumi panu.*+ 19 Muziphunzitsa ana anu mawu amenewa, ndipo muzilankhula nawo mawuwa mukakhala pansi mʼnyumba mwanu, mukamayenda pamsewu, mukamagona komanso mukadzuka.+

  • Yoswa 4:6, 7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Miyalayo idzakhala chizindikiro kwa inu. Ana anu* akamadzafunsa mʼtsogolo muno kuti, ‘Kodi miyalayi ndi ya chiyani?’+ 7 Muzidzawauza kuti: ‘Nʼchifukwa chakuti madzi amumtsinje wa Yorodano anagawikana chifukwa cha likasa+ la pangano la Yehova. Likasalo likudutsa mumtsinje wa Yorodano, madzi a mtsinjewo anagawikana. Miyalayi ndi yoti izikumbutsa Aisiraeli zimenezo mpaka kalekale.’”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena