Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 11:31-34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Kenako Yehova anabweretsa mphepo yamphamvu kuchokera kunyanja. Mphepoyo inabweretsa zinziri, ndipo inazimwaza kuzungulira msasawo+ mpaka pamtunda woyenda tsiku limodzi kulowera mbali zonse za msasawo. Inazimwaza kuzungulira msasawo, moti zinaunjikana mulu wokwana pafupifupi masentimita 90* kuchokera pansi. 32 Ndiyeno anthuwo anayamba kugwira zinzirizo. Anazigwira masana onse, usiku wonse, mpakanso tsiku lotsatira osapuma. Palibe amene anagwira zosakwana mahomeri* 10 ndipo ankaziyanika paliponse, moti zinangoti mbwee, pamsasa wonsewo. 33 Koma nyamayo idakali mʼkamwa mwawo, asanaitafune nʼkomwe, mkwiyo wa Yehova unayakira anthuwo. Ndipo Yehova anayamba kuwalanga moti anthu ambiri anaphedwa.+

      34 Malo amenewo anawatchula kuti Kibiroti-hatava,*+ chifukwa anakwirirapo anthu amene anasonyeza mtima wadyera.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena