Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 7:23, 24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Koma ndinawalamula kuti: “Muzimvera mawu anga, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu, inuyo mudzakhala anthu anga.+ Muziyenda mʼnjira imene ndakulamulani, kuti zinthu zikuyendereni bwino.”’+ 24 Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu.+ Mʼmalomwake, anayenda motsatira zofuna zawo. Mouma khosi anatsatira zofuna za mtima wawo woipawo,+ moti anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo,

  • Yeremiya 11:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Inetu ndinkalangiza makolo anu pa tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Iguputo ndipo ndikupitiriza mpaka pano. Ndinkawalangiza mobwerezabwereza* kuti: “Muzimvera mawu anga.”+ 8 Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu. Mʼmalomwake aliyense wa iwo anapitiriza kuumitsa mtima wake ndi kuchita zofuna za mtima wake woipawo.+ Choncho ndinawalanga mogwirizana ndi mawu onse a mʼpangano langa limene ndinawalamula kuti azilitsatira koma iwo anakana kulitsatira.’”

  • Mika 6:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Mukutsatira malamulo a Omuri komanso zinthu zonse zimene anthu a mʼnyumba ya Ahabu amachita.+

      Ndipo mukuyendera malangizo awo.

      Nʼchifukwa chake ndidzakusandutsani chinthu chodabwitsa,

      Ndipo anthu amumzindawo adzakhala oyenera kuwaimbira mluzu.+

      Inuyo mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena