-
Yeremiya 25:31-33Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 ‘Phokoso lidzamveka kumalekezero a dziko lapansi,
Chifukwa Yehova akufuna kuimba mlandu mitundu ya anthu.
Iye adzapereka yekha chiweruzo kwa anthu onse.+
Ndipo anthu oipa adzawapha ndi lupanga,’ akutero Yehova.
32 Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti:
‘Taonani! Tsoka likufalikira kuchokera ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,+
Ndipo mkuntho wamphamvu udzafika kuchokera kumadera akutali kwambiri a dziko lapansi.+
33 Pa tsiku limenelo anthu amene adzaphedwe ndi Yehova adzachokera kumalekezero a dziko lapansi kukafika kumalekezero ena a dziko lapansi. Maliro awo sadzaliridwa, sadzawasonkhanitsa pamodzi kapena kuwaika mʼmanda. Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.’
-