Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 23:26-28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Kenako Sauli anafika mbali ina ya phiri limene Davide ndi amuna amene anali naye anabisala. Zitatero Davide anayamba kukonzeka mwamsanga kuti athawe+ Sauli. Pa nthawiyi nʼkuti Sauli ndi asilikali ake atatsala pangʼono kupeza Davide ndi amuna amene anali naye.+ 27 Koma kenako kunabwera munthu ndi uthenga wakuti: “Bwerani mofulumira, Afilisiti aukira dziko lathu!” 28 Zitatero Sauli anasiya kusakasaka Davide+ ndipo anabwerera kukamenyana ndi Afilisiti. Nʼchifukwa chake malowo anawapatsa dzina lakuti Thanthwe Logawanitsa.

  • 2 Samueli 17:21, 22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Anthuwo atachoka, Ahimazi ndi Yonatani anatuluka mʼchitsimemo nʼkupita kukauza Mfumu Davide kuti: “Nyamukani mwamsanga ndipo muwoloke mtsinje.” Kenako anawauza malangizo amene Ahitofeli anapereka.+ 22 Nthawi yomweyo Davide ananyamuka pamodzi ndi anthu onse amene anali naye, ndipo anawoloka Yorodano. Pofika mʼbandakucha, aliyense anali atawoloka Yorodano.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena