-
Yesaya 61:1-3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
61 Mzimu wa Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, uli pa ine,+
Chifukwa Yehova anandidzoza kuti ndilengeze uthenga wabwino kwa anthu ofatsa.+
Anandituma kuti ndikamange mabala a anthu osweka mtima,
Kuti ndilengeze za ufulu kwa anthu amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina,
Komanso kuti maso a akaidi adzatsegulidwa.+
2 Wandituma kuti ndilengeze za chaka cha Yehova chokomera anthu mtima,*
Ndi za tsiku lobwezera la Mulungu wathu,+
Komanso kuti nditonthoze anthu onse amene akulira,+
3 Kuti ndisamalire anthu onse amene akulirira Ziyoni,
Kuti ndiwapatse nsalu yovala kumutu mʼmalo mwa phulusa,
Kuti ndiwapatse mafuta kuti azisangalala mʼmalo molira,
Kuti ndiwapatse chovala choti azivala ponditamanda mʼmalo mokhala otaya mtima.
-