12 Inu Yehova, ndikabweretsa dandaulo langa kwa inu,
Komanso ndikamalankhula ndi inu nkhani zokhudza chilungamo, mumasonyeza kuti ndinu wolungama.+
Koma nʼchifukwa chiyani anthu oipa, zinthu zikuwayendera bwino,+
Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu amene amachita zachinyengo amakhala opanda nkhawa?