Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 5:20-22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Gehazi,+ mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu woona,+ anaganiza mumtima mwake kuti: ‘Zoona mbuyanga wangomusiya Namani wa ku Siriya+ uja osalandira zinthu zomwe anabweretsa? Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wamoyo, ndimʼthamangira kuti ndikatengeko zinthu zina.’ 21 Gehazi anathamangiradi Namani ndipo Namani ataona kuti munthu akumʼthamangira, anatsika pagaleta lake kuti akumane naye. Kenako anati: “Nʼkwabwino?” 22 Gehazi anayankha kuti: “Inde nʼkwabwino. Mbuyanga wandituma kuti, ‘Posachedwapa kwabwera anyamata awiri, ana a aneneri, kuchokera kudera lamapiri la Efuraimu. Muwapatseko talente imodzi ya siliva ndi zovala ziwiri.’”+

  • Yeremiya 17:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo,*+

      Ali ngati nkhwali imene imasonkhanitsa mazira amene sinaikire.

      Chuma chakecho chidzatha asanakwanitse hafu ya zaka za moyo wake,

      Ndipo pamapeto pake adzadziwika kuti ndi wopusa.”

  • 1 Timoteyo 6:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Koma anthu ofunitsitsa kulemera amakumana ndi mayesero ndiponso amakodwa mumsampha.+ Iwo amalakalaka zinthu zowapweteketsa komanso amachita zinthu mopanda nzeru. Zimenezi zimawawononga ndiponso kuwabweretsera mavuto.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena