Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 13:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiye ndinaganiza kuti, ‘Afilisitiwa abwera ku Giligala kuno kudzamenyana nane, ndipo sindinakhazike pansi mtima wa Yehova.’ Choncho ndinaona kuti ndiyenera kupereka nsembe yopsereza.”

      13 Koma Samueli anauza Sauli kuti: “Zimene wachitazi ndi zopusa. Sunamvere lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.+ Ukanamvera, Yehova akanachititsa kuti banja lako lilamulire Isiraeli mpaka kalekale.

  • 1 Samueli 15:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Samueli anati: “Kodi Yehova amasangalala ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina+ kuposa kumvera mawu a Yehova? Dikira ndikuuze! Kumvera kumaposa nsembe,+ ndipo kumvetsera mosamala kumaposa mafuta+ a nkhosa zamphongo.

  • Miyambo 21:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Nsembe ya munthu woipa ndi yonyansa.+

      Ndiye kuli bwanji akaipereka ndi zolinga zoipa!*

  • Yesaya 1:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Musabweretsenso nsembe zina za mbewu zomwe ndi zopanda phindu.

      Zofukiza zanu ndi zonyansa kwa ine.+

      Mumachita zikondwerero mwezi watsopano ukaoneka,+ mumasunga masabata,+ ndiponso mumaitanitsa misonkhano.+

      Komanso ine ndatopa kukuonani mukugwiritsira ntchito mphamvu zamatsenga+ mukamachita msonkhano wanu wapadera.

  • Hoseya 6:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Chifukwa ndimakondwera ndi chikondi chokhulupirika,* osati nsembe.

      Ndimakondweranso ndi kudziwa Mulungu, osati nsembe zopsereza zathunthu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena