11 Taona! Onse amene amakupsera mtima adzachita manyazi ndipo adzanyozeka.+
Anthu amene akumenyana nawe adzawonongedwa ndipo adzatha.+
12 Anthu amene akulimbana nawe udzawafunafuna koma sudzawapeza.
Anthu amene akumenyana nawe adzakhala ngati chinthu chimene kulibeko ndipo sadzakhalanso ngati kanthu.+