Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ezekieli 18:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Sazunza munthu aliyense+ koma amabweza chikole kwa munthu amene anakongola zinthu zake.+ Salanda zinthu za ena mwauchifwamba+ koma amapereka chakudya chake kwa munthu amene ali ndi njala+ ndiponso amaphimba munthu wamaliseche ndi chovala.+ 8 Iye sauza anthu kuti amupatse chiwongoladzanja akabwereketsa zinthu ndipo sakongoza zinthu mwa katapira+ koma amapewa kuchita zinthu mopanda chilungamo.+ Iye amatsatira chilungamo chenicheni akamaweruza munthu ndi mnzake.+

  • Yakobo 2:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ngati mʼbale kapena mlongo alibe zovala* komanso chakudya chokwanira pa tsikulo, 16 koma wina mwa inu nʼkumuuza kuti, “Uyende bwino, upeze zovala ndi zakudya za tsiku lililonse,” koma osamupatsa zimene akufunikirazo kuti akhale ndi moyo, kodi pali phindu lanji?+

  • 1 Yohane 3:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Aliyense amene ali ndi zinthu zofunika pa moyo ndipo akuona mʼbale wake akuvutika chifukwa chosowa zinthuzo, koma osamusonyeza chifundo, kodi tingati munthu ameneyu amakonda Mulungu?+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena