-
Yeremiya 35:15Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Ndinkakutumizirani mobwerezabwereza*+ atumiki anga onse omwe anali aneneri. Ndinkawauza uthenga wakuti, ‘Chonde bwererani ndipo aliyense asiye njira zake zoipa.+ Muzichita zinthu zabwino. Musatsatire milungu ina nʼkumaitumikira. Mukatero mudzapitiriza kukhala mʼdziko limene ndinapatsa inuyo ndi makolo anu.’+ Koma inu simunatchere khutu kapena kundimvera.
-