10 Koma iwe Yakobo mtumiki wanga usachite mantha,” akutero Yehova,
“Ndipo iwe Isiraeli usaope.+
Chifukwa ndidzakupulumutsa kuchokera kutali
Ndidzapulumutsanso ana ako kuchokera kudziko limene anatengedwa kukakhala akapolo.+
Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala mosatekeseka komanso mopanda zosokoneza.
Sipadzakhala wowaopseza.+