-
Yeremiya 51:7Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
7 Babulo anali ngati kapu yagolide mʼdzanja la Yehova.
Anachititsa kuti dziko lonse lapansi liledzere.
-
-
Danieli 5:18, 19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
18 Inu mfumu, Mulungu Wamʼmwambamwamba anapatsa bambo anu Nebukadinezara ufumu, ukulu, ulemu ndi ulemerero.+ 19 Chifukwa chakuti Mulungu anamupatsa ukulu umenewu, anthu a mitundu yonse komanso anthu olankhula zinenero zosiyanasiyana ankanjenjemera chifukwa cha mantha pamaso pake.+ Aliyense amene ankafuna kumupha ankamupha, amene ankafuna kumusiya ndi moyo ankamusiya ndipo aliyense amene ankafuna kumukweza ankamukweza, amene ankafuna kumutsitsa ankamutsitsa.+
-