24 Choncho Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Anthu anga amene mukukhala mʼZiyoni, musachite mantha chifukwa cha Msuri amene ankakukwapulani ndi chikwapu+ ndiponso kukumenyani ndi ndodo, ngati mmene ankachitira Iguputo.+