-
Yeremiya 25:9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 ndikuitana mafuko onse akumpoto,”+ akutero Yehova, “ndikuitananso Mfumu Nebukadinezara* ya ku Babulo, mtumiki wanga.+ Ndibweretsa anthu amenewa kuti aukire dziko lino+ ndi anthu amene akukhala mmenemo komanso mitundu yonse imene yakuzungulirani.+ Ndidzakuwonongani inuyo ndi mitundu yonse yokuzungulirani ndipo ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha chimene anthu azidzachiimbira mluzu ndipo malo anu adzakhala mabwinja mpaka kalekale.
-
-
Ezekieli 29:19, 20Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Ine ndikupereka dziko la Iguputo kwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo.+ Iye adzatenga chuma cha dzikolo komanso kulanda zinthu zake zochuluka. Zimenezi zidzakhala malipiro a asilikali ake.
20 Ndimupatsa dziko la Iguputo monga chipukutamisozi pa ntchito imene anagwira pomenyana ndi Turo, chifukwa iwo anachita zimene ine ndinkafuna,’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.
-