Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 14:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndiyeno Yehova anandiyankha kuti: “Aneneriwo akulosera zinthu zabodza mʼdzina langa.+ Ine sindinawatume, kuwalamula kapena kulankhula nawo.+ Maulosi amene akukuuzaniwo ndi masomphenya abodza, maulosi opanda pake ndi chinyengo chamumtima mwawo.+

  • Yeremiya 28:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Kenako mneneri Yeremiya anauza mneneri Hananiya+ kuti: “Tamvera iwe Hananiya! Yehova sanakutume, koma iwe wachititsa anthuwa kukhulupirira zinthu zabodza.+ 16 Choncho Yehova wanena kuti, ‘Ndikukuchotsera moyo wako. Chaka chomwe chino iweyo ufa, chifukwa walimbikitsa anthu kuti apandukire Yehova.’”+

  • Ezekieli 13:8, 9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “‘Chifukwa choti mwalankhula zabodza ndipo masomphenya anu ndi onama, ine ndithana nanu,’ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.”+ 9 Dzanja langa likulimbana ndi aneneri amene masomphenya awo ndi abodza ndiponso amene akulosera zonama.+ Iwo sadzakhala mʼgulu la anthu amene ndimawakonda ndipo sadzalembedwa mʼbuku la mayina a anthu a nyumba ya Isiraeli. Komanso sadzabwerera kudziko la Isiraeli ndipo mudzadziwa kuti ine ndine Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena