Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 33:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Ndidzawayeretsa ku zolakwa zonse zimene anandichimwira+ ndipo ndidzawakhululukira zolakwa zawo zonse zimene anandichimwira nʼkuphwanya nazo malamulo anga.+

  • Yeremiya 50:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 “Mʼmasiku amenewo ndiponso pa nthawi imeneyo,

      Cholakwa cha Isiraeli chidzafufuzidwa,

      Koma sichidzapezeka,” akutero Yehova.

      “Machimo a Yuda sadzapezeka,

      Chifukwa ine ndidzakhululukira anthu amene ndidzawasiye ndi moyo.”+

  • Mateyu 26:27, 28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Kenako anatenga kapu ya vinyo ndipo atayamika, anaipereka kwa iwo nʼkunena kuti: “Imwani nonsenu.+ 28 Vinyoyu akuimira ‘magazi anga+ a pangano,’+ amene adzakhetsedwe chifukwa cha anthu ambiri+ kuti machimo awo akhululukidwe.+

  • Aheberi 8:10-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “‘Pangano limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili: Ndidzaika malamulo anga mʼmaganizo mwawo ndiponso kuwalemba mʼmitima yawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,’+ akutero Yehova.*

      11 ‘Munthu sadzaphunzitsanso nzika inzake kapena mʼbale wake kuti, “Mumʼdziwe Yehova!”* Chifukwa aliyense adzandidziwa kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. 12 Ine ndidzawachitira chifundo pa zochita zawo zosalungama, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.’”+

  • Aheberi 9:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Ndiye chifukwa chake iye ndi mkhalapakati wa pangano latsopano+ kuti anthu amene aitanidwa alandire lonjezo la moyo wosatha.+ Izi zatheka chifukwa cha imfa yake, imene inali ngati dipo lowamasula+ ku machimo amene iwo anali nawo mʼpangano lakale lija.

  • Aheberi 10:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Kenako unanenanso kuti: “Ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo komanso zochita zawo zosonyeza kusamvera malamulo.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena