Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 23:8, 9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Kenako inaitanitsa ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda. Ndipo malo okwezeka amene ansembewo ankaperekako nsembe yautsi, kuyambira ku Geba+ mpaka ku Beere-seba,+ inawachititsa kuti akhale osayenera kulambirako. Inagwetsanso malo okwezeka a pageti amene anali pakhomo lapageti la Yoswa mkulu wa mzindawo. Getilo linali mbali ya kumanzere munthu akamalowa pageti la mzindawo. 9 Ansembe a malo okwezekawo sankatumikira kuguwa lansembe la Yehova ku Yerusalemu.+ Koma ankadya mikate yopanda zofufumitsa limodzi ndi abale awo.

  • 2 Mbiri 29:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Hezekiya+ anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 29. Mayi ake dzina lawo linali Abiya mwana wa Zekariya.+

  • 2 Mbiri 29:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Ndiyeno anawauza kuti: “Tamverani Alevi inu. Dziyeretseni+ ndipo muyeretsenso nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse mʼmalo oyera chinthu chilichonse chodetsedwa.+

  • Nehemiya 9:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Mafumu athu, akalonga athu, ansembe athu ndi makolo athu sanatsatire Chilamulo chanu ndipo sanamvere malamulo anu kapena zikumbutso zanu zowachenjeza.

  • Yeremiya 23:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Aneneri ndi ansembe, onse aipitsidwa.*+

      Ndipo ngakhale mʼnyumba mwanga ndapezamo zoipa zimene akuchita,”+ akutero Yehova.

  • Ezekieli 8:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Kenako iye anandiuza kuti: “Iwe mwana wa munthu, kweza maso ako uyangʼane kumpoto.” Choncho ndinakweza maso anga nʼkuyangʼana kumpoto, ndipo ndinaona kuti kumpoto kwa geti la guwa lansembe kunali fano loimira nsanje lija pakhomo la getilo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena