13 Iweyo wanena mumtima mwako kuti, ‘Ndikwera kumwamba.+
Ndikweza mpando wanga wachifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu,+
Ndipo ndikhala paphiri lokumanapo
Kumapeto kwenikweni kwa madera akumpoto.+
14 Ndikwera pamwamba kupitirira nsonga za mitambo.
Ndidzipanga kukhala wofanana ndi Wamʼmwambamwamba.’