-
Maliko 3:31-35Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 Tsopano panafika mayi ake ndi azichimwene ake+ ndipo anaima panja nʼkutuma munthu kuti akamuitane.+ 32 Gulu la anthu linakhala momuzungulira ndipo anthuwo anamuuza kuti: “Mayi anu ndi azichimwene anu ali panjapa akukufunani.”+ 33 Koma iye anawayankha kuti: “Kodi mayi anga ndi azichimwene anga ndi ndani?” 34 Kenako anayangʼana onse amene anakhala pansi momuzungulira aja nʼkunena kuti: “Onani! Mayi anga ndi azichimwene anga ndi awa.+ 35 Aliyense amene amachita zimene Mulungu amafuna, ameneyo ndi mchimwene wanga, mchemwali wanga ndi mayi anga.”+
-