Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 16:5-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Kenako ophunzira ake anawolokera kutsidya lina koma anaiwala kutenga mikate.+ 6 Ndiyeno Yesu anawauza kuti: “Khalani maso ndipo musamale ndi chofufumitsa cha Afarisi ndi Asaduki.”+ 7 Koma iwo anayamba kukambirana kuti: “Sitinatenge mikate pobwera kuno.” 8 Yesu anadziwa zimenezi ndipo ananena kuti: “Achikhulupiriro chochepa inu, nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe mikate? 9 Kodi mfundo yake simukuimvetsabe? Kapena kodi simukukumbukira anthu 5,000 amene anadya mitanda 5 ya mikate, komanso kuchuluka kwa madengu amene munatolera a chakudya chimene chinatsala?+ 10 Kapena kodi simukukumbukira anthu 4,000 amene anadya mitanda 7 ya mikate, komanso kuchuluka kwa madengu akuluakulu a chakudya chimene chinatsala amene munatolera?+ 11 Nanga bwanji simukuzindikira kuti sindikunena za mkate, koma zakuti musamale ndi zofufumitsa za Afarisi ndi Asaduki?”+ 12 Atatero anazindikira kuti sakunena zakuti asamale ndi zofufumitsa za mkate, koma kuti asamale ndi zimene Afarisi ndi Asaduki amaphunzitsa.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena