Mateyu 16:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kuuza ophunzira ake kuti iyeyo akuyenera kupita ku Yerusalemu. Kumeneko akazunzidwa kwambiri ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi ndipo akaphedwa, koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.+ Mateyu 17:22, 23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Yesu anawauza kuti: “Mwana wa munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu+ 23 ndipo adzamupha. Koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.”+ Atamva zimenezi iwo anamva chisoni kwambiri. Maliko 8:31 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 Komanso anayamba kuwaphunzitsa kuti Mwana wa munthu akuyenera kukumana ndi mavuto ambiri ndiponso kukanidwa ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi. Ndipo adzaphedwa+ nʼkuukitsidwa patapita masiku atatu.+ Luka 9:44, 45 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 44 “Mvetserani mosamala ndipo muzikumbukira mawu awa, chifukwa Mwana wa munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”+ 45 Koma ophunzirawo sanamvetse zimene anawauzazo. Tanthauzo lake linali lobisika kwa iwo kuti asazindikire ndipo ankaopa kumufunsa za mawu amenewa.
21 Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kuuza ophunzira ake kuti iyeyo akuyenera kupita ku Yerusalemu. Kumeneko akazunzidwa kwambiri ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi ndipo akaphedwa, koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.+
22 Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Yesu anawauza kuti: “Mwana wa munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu+ 23 ndipo adzamupha. Koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.”+ Atamva zimenezi iwo anamva chisoni kwambiri.
31 Komanso anayamba kuwaphunzitsa kuti Mwana wa munthu akuyenera kukumana ndi mavuto ambiri ndiponso kukanidwa ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi. Ndipo adzaphedwa+ nʼkuukitsidwa patapita masiku atatu.+
44 “Mvetserani mosamala ndipo muzikumbukira mawu awa, chifukwa Mwana wa munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”+ 45 Koma ophunzirawo sanamvetse zimene anawauzazo. Tanthauzo lake linali lobisika kwa iwo kuti asazindikire ndipo ankaopa kumufunsa za mawu amenewa.