Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 14:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Wansembe azipita kunja kwa msasa kukamuona. Ngati munthuyo wachira khate lake, 4 wansembe azimulamula kuti abweretse mbalame zamoyo ziwiri zosadetsedwa, nthambi ya mtengo wa mkungudza, ulusi wofiira kwambiri ndi kamtengo ka hisope* kuti adzazigwiritse ntchito pomuyeretsa.+

  • Levitiko 14:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Pa tsiku la 8, iye adzatenge nkhosa zazingʼono zamphongo ziwiri zopanda chilema komanso nkhosa yaingʼono yaikazi+ imodzi yopanda chilema, yosapitirira chaka chimodzi. Adzatengenso ufa wosalala wokwana magawo atatu mwa magawo 10 a muyezo wa efa,* monga nsembe yake ya mbewu+ yothira mafuta ndi muyezo umodzi* wa mafuta.+ 11 Ndipo wansembe amene wagamula kuti munthuyo ndi woyera, azionetsa amene akudziyeretsayo, limodzi ndi zinthu zakezo kwa Yehova, pakhomo la chihema chokumanako.

  • Deuteronomo 24:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Ngati kwabuka matenda a khate,* muzionetsetsa kuti mukuchita zinthu zonse mogwirizana ndi zimene Alevi omwe ndi ansembe akulangizani.+ Muzionetsetsa kuti mukuchita mogwirizana ndi zimene ndinawalamula.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena