7 Chifukwa nyumba ya Isiraeli ndi munda wa mpesa wa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+
Amuna a ku Yuda ndi mitengo ya mpesa imene ankaikonda kwambiri.
Iye ankayembekezera chilungamo,+
Koma pankachitika zinthu zopanda chilungamo.
Ankayembekezera zinthu zolungama
Koma ankangomva anthu akulira chifukwa chozunzidwa.”+