30 Kunena zoona, Yesu anachitanso zizindikiro zina zambiri pamaso pa ophunzirawo, zimene sizinalembedwe mumpukutu uno.+ 31 Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, komanso chifukwa choti mwakhulupirira, mukhale ndi moyo mʼdzina lake.+