Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 9:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Nthawi inayake, pamene ankadya chakudya* mʼnyumba ina, kunabwera anthu ambiri okhometsa msonkho komanso ochimwa ndipo anayamba kudya* limodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake.+ 11 Koma Afarisi ataona zimenezi anafunsa ophunzira ake kuti: “Nʼchifukwa chiyani mphunzitsi wanu amadya limodzi ndi anthu okhometsa msonkho komanso ochimwa?”+

  • Maliko 2:15, 16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Nthawi inayake, ankadya chakudya* mʼnyumba mwa Levi ndipo anthu ambiri okhometsa msonkho komanso ochimwa ankadya limodzi ndi Yesu ndiponso ophunzira ake. Kumeneko kunali anthu ambiri amene ankamutsatira.+ 16 Koma alembi a Afarisi, ataona kuti Yesu akudya limodzi ndi anthu ochimwa ndi okhometsa msonkho, anayamba kufunsa ophunzira ake kuti: “Bwanji akudya limodzi ndi okhometsa msonkho komanso anthu ochimwa?”

  • Luka 5:29, 30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Kenako Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu kunyumba kwake. Kumeneko kunabwera anthu ambiri okhometsa msonkho komanso ochimwa ndipo ankadya* limodzi ndi Yesu komanso ophunzira ake.+ 30 Afarisi ndi alembi awo ataona izi, anayamba kungʼungʼudza nʼkufunsa ophunzira ake kuti: “Nʼchifukwa chiyani inu mumadya ndi kumwa limodzi ndi okhometsa msonkho komanso anthu ochimwa?”+

  • 1 Timoteyo 1:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Mawu akuti Khristu Yesu anabwera mʼdziko kudzapulumutsa ochimwa,+ ndi mawu oona komanso oyenera kuwavomereza ndi mtima wonse. Pa ochimwa amenewa, ine ndiye wochimwa kwambiri.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena