-
Machitidwe 9:39, 40Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
39 Petulo atamva zimenezi, ananyamuka nʼkupita nawo limodzi. Atafika, anamutenga nʼkupita naye mʼchipinda chamʼmwamba chija. Akazi onse amasiye anabwera kwa iye akulira ndipo ankamuonetsa zovala zambiri ndiponso mikanjo imene Dorika ankasoka pamene anali nawo. 40 Petulo anauza anthu onse kuti atuluke,+ ndiyeno anagwada nʼkupemphera. Kenako anatembenuka nʼkuyangʼana mtembowo nʼkunena kuti: “Tabita, dzuka!” Ndiyeno mayiyo anatsegula maso ndipo ataona Petulo, anadzuka nʼkukhala tsonga.+
-