Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 12:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Pomaliza, Samueli anauza Aisiraeli onse kuti: “Ndachita zonse zimene* munandiuza, ndipo ndakusankhirani mfumu yoti izikulamulirani.+

  • 1 Samueli 12:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ine ndaima pano. Mupereke umboni pamaso pa Yehova ndi pamaso pa wodzozedwa wake:+ Kodi alipo amene ndinamʼtengera ngʼombe kapena bulu wake?+ Nanga alipo amene ndinamʼchitirapo zachinyengo kapena kumʼpondereza? Kodi ndinalandirapo chiphuphu kwa aliyense kuti ndisachite chilungamo?+ Ngati ndinachitapo zimenezi, ndine wokonzeka kukubwezerani.”+

  • Mateyu 10:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Muzichiritsa odwala,+ kuukitsa anthu akufa, kuyeretsa akhate komanso kutulutsa ziwanda. Munalandira kwaulere, muzipereka kwaulere.

  • 1 Akorinto 9:11, 12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ngati tinakupatsani zinthu zauzimu,* kodi nʼkulakwa kulandira* zinthu zofunika pa moyo kuchokera kwa inu?+ 12 Ngati anthu ena amayembekezera kuti muwachitire zimenezi, ndiye kuli bwanji ifeyo? Komatu ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewo.+ Koma timapirira zinthu zonse kuti tisalepheretse ena kumva uthenga wabwino wonena za Khristu.+

  • 2 Akorinto 7:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Titsegulireni mitima yanu.*+ Ifetu sitinalakwire aliyense, sitinaipitse aliyense ndipo sitinadyere aliyense masuku pamutu.+

  • Tito 1:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Popeza ndi mtumiki* wa Mulungu, woyangʼanira ayenera kukhala wopanda chifukwa chomunenezera. Asakhale womva zake zokha,+ wa mtima wapachala,+ womwa mowa mwauchidakwa, wankhanza* kapena wokonda kupeza phindu mwachinyengo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena