17 Abulamu ali ndi zaka 99, Yehova anaonekera kwa iye nʼkumuuza kuti: “Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse. Uziyenda mʼnjira zanga ndipo ukhale wopanda cholakwa. 2 Ndidzakhazikitsa pangano langa pakati pa ine ndi iwe+ ndipo ndidzachulukitsa kwambiri mbadwa zako.”+