Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 23
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Anthu osayenera kulowa mumpingo wa Mulungu (1-8)

      • Ukhondo mumsasa (9-14)

      • Kapolo amene wathawa kwa mbuye wake (15, 16)

      • Uhule unaletsedwa (17, 18)

      • Chiwongoladzanja komanso malonjezo (19-23)

      • Zimene anthu ongodutsa ankaloledwa kudya (24, 25)

Deuteronomo 23:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 21:18, 20; Yes 56:4, 5

Deuteronomo 23:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:14; Le 20:10

Deuteronomo 23:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ne 13:1, 2

Deuteronomo 23:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Owe 11:18
  • +Nu 22:6; Yos 24:9

Deuteronomo 23:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 22:35
  • +Nu 23:11, 25; 24:10
  • +De 7:7, 8

Deuteronomo 23:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Sa 8:2; 12:31

Deuteronomo 23:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 25:25, 26; 36:1; Nu 20:14
  • +Ge 46:6; Le 19:34; Sl 105:23

Deuteronomo 23:9

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “choipa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 21:5; 2Sa 11:11

Deuteronomo 23:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 15:16

Deuteronomo 23:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 15:31

Deuteronomo 23:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Chimenechi ndi chimbudzi.

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/1/2012, tsa. 6

    Chinsinsi cha Banja, ptsa. 46-47

Deuteronomo 23:13

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/1/2012, tsa. 6

    Chinsinsi cha Banja, ptsa. 46-47

    Galamukani!,

    12/8/1991, tsa. 22

Deuteronomo 23:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 26:12
  • +1Pe 1:16

Deuteronomo 23:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:21

Deuteronomo 23:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:29; 21:9
  • +1Mf 14:24; 2Mf 23:7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, tsa. 29

    4/15/1989, tsa. 3

Deuteronomo 23:18

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “galu.”

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, tsa. 29

    4/15/1989, tsa. 3

Deuteronomo 23:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:25; Le 25:36, 37; Ne 5:10; Sl 15:5

Deuteronomo 23:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 15:6
  • +Miy 28:8
  • +De 15:4, 7, 10; Miy 19:17; Lu 6:34, 35

Deuteronomo 23:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Owe 11:30, 31; 1Sa 1:11
  • +Yon 2:9
  • +Mla 5:4, 6

Deuteronomo 23:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mla 5:5

Deuteronomo 23:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 30:2; Sl 15:4; Miy 20:25
  • +Owe 11:35; 1Sa 14:24; Mt 5:33

Deuteronomo 23:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 6:11; Aro 13:10

Deuteronomo 23:25

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 12:1; Lu 6:1

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 23:1Le 21:18, 20; Yes 56:4, 5
Deut. 23:2Eks 20:14; Le 20:10
Deut. 23:3Ne 13:1, 2
Deut. 23:4Owe 11:18
Deut. 23:4Nu 22:6; Yos 24:9
Deut. 23:5Nu 22:35
Deut. 23:5Nu 23:11, 25; 24:10
Deut. 23:5De 7:7, 8
Deut. 23:62Sa 8:2; 12:31
Deut. 23:7Ge 25:25, 26; 36:1; Nu 20:14
Deut. 23:7Ge 46:6; Le 19:34; Sl 105:23
Deut. 23:91Sa 21:5; 2Sa 11:11
Deut. 23:10Le 15:16
Deut. 23:11Le 15:31
Deut. 23:14Le 26:12
Deut. 23:141Pe 1:16
Deut. 23:16Eks 22:21
Deut. 23:17Le 19:29; 21:9
Deut. 23:171Mf 14:24; 2Mf 23:7
Deut. 23:19Eks 22:25; Le 25:36, 37; Ne 5:10; Sl 15:5
Deut. 23:20De 15:6
Deut. 23:20Miy 28:8
Deut. 23:20De 15:4, 7, 10; Miy 19:17; Lu 6:34, 35
Deut. 23:21Owe 11:30, 31; 1Sa 1:11
Deut. 23:21Yon 2:9
Deut. 23:21Mla 5:4, 6
Deut. 23:22Mla 5:5
Deut. 23:23Nu 30:2; Sl 15:4; Miy 20:25
Deut. 23:23Owe 11:35; 1Sa 14:24; Mt 5:33
Deut. 23:24Mt 6:11; Aro 13:10
Deut. 23:25Mt 12:1; Lu 6:1
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 23:1-25

Deuteronomo

23 “Mwamuna amene anafulidwa pophwanya mavalo ake kapena amene anadulidwa maliseche asamalowe mumpingo wa Yehova.+

2 Mwana wapathengo asamalowe mumpingo wa Yehova.+ Ngakhale mpaka mʼbadwo wa 10, mbadwa zake zisamalowe mumpingo wa Yehova.

3 Mbadwa ya Amoni kapena Mowabu isamalowe mumpingo wa Yehova.+ Ngakhale mpaka mʼbadwo wa 10, mbadwa zawo zisadzalowe mumpingo wa Yehova mpaka kalekale, 4 chifukwa chakuti sanakuthandizeni pokupatsani chakudya ndi madzi pamene munali pa ulendo mutatuluka mu Iguputo,+ komanso chifukwa chakuti analemba ganyu Balamu mwana wa Beori, amene kwawo ndi ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni.+ 5 Koma Yehova Mulungu wanu anakana kumvera Balamu.+ Mʼmalomwake, Yehova Mulungu wanu anakusinthirani temberero kukhala dalitso,+ chifukwa Yehova Mulungu wanu anakukondani.+ 6 Musamachite chilichonse powathandiza kuti azikhala mwamtendere komanso kuti zinthu ziwayendere bwino masiku onse a moyo wanu.+

7 Musamadane ndi mbadwa ya Edomu, chifukwa ndi mʼbale wanu.+

Musamadane ndi munthu wa ku Iguputo, chifukwa munali alendo mʼdziko lawo.+ 8 Ana awo a mʼbadwo wachitatu angathe kulowa mumpingo wa Yehova.

9 Mukamanga msasa kuti mumenyane ndi adani anu, muzipewa chilichonse chodetsa.*+ 10 Ngati mwamuna wadetsedwa chifukwa chotulutsa umuna usiku,+ azipita kunja kwa msasa ndipo asamalowenso mumsasamo. 11 Ndiyeno madzulo azisamba ndi madzi ndipo kenako angathe kubwerera kumsasa dzuwa likalowa.+ 12 Muzikhala ndi malo apadera* kunja kwa msasa, kumene muzipita mukafuna kudzithandiza. 13 Pa zida zanu pazikhalanso chokumbira. Ndiyeno mukafuna kudzithandiza kunja kwa msasa, muzikumba dzenje ndi chokumbiracho ndipo mukamaliza muzikwirira zoipazo. 14 Chifukwa Yehova Mulungu wanu akuyendayenda mumsasa wanu+ kuti akupulumutseni ndi kupereka adani anu mʼmanja mwanu. Choncho msasa wanu uzikhala woyera,+ kuti asaone choipa chilichonse pakati panu nʼkusiya kuyenda nanu limodzi.

15 Kapolo akathawa kwa mbuye wake nʼkubwera kwa inu, musamamubweze kwa mbuye wakeyo. 16 Iye azikhala pakati panu pamalo alionse amene angasankhe mu umodzi mwa mizinda yanu, kulikonse kumene wakonda. Ndipo musamamuzunze.+

17 Mwana wamkazi aliyense wa Chiisiraeli asakhale hule wapakachisi,+ ndiponso mwana wamwamuna aliyense wa Chiisiraeli asakhale hule wapakachisi.+ 18 Musamabweretse malipiro a hule lalikazi kapena malipiro a hule lalimuna* mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kuti mukwaniritse lonjezo lililonse, chifukwa malipiro onsewo ndi onyansa kwa Yehova Mulungu wanu.

19 Mʼbale wanu musamamulipiritse chiwongoladzanja pa ndalama,+ chakudya kapena pa chilichonse chimene munthu angafunepo chiwongoladzanja. 20 Mlendo mungamulipiritse chiwongoladzanja,+ koma mʼbale wanu musamamulipiritse chiwongoladzanja,+ kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa chilichonse chimene mukuchita mʼdziko limene mukupita kukalitenga kuti likhale lanu.+

21 Mukalonjeza kanthu kwa Yehova Mulungu wanu+ musamachedwe kukwaniritsa zimene mwalonjezazo.+ Chifukwa Yehova Mulungu wanu adzafuna ndithu kuti mukwaniritse zimene mwalonjezazo. Mukapanda kutero mudzakhala kuti mwachimwa.+ 22 Koma mukapanda kulonjeza, simudzachimwa.+ 23 Muzisunga mawu a pakamwa panu+ ndipo muzikwaniritsa zimene munalonjeza ndi pakamwa panu monga nsembe yaufulu yoperekedwa kwa Yehova Mulungu wanu.+

24 Mukalowa mʼmunda wa mpesa wa mnzanu mungathe kudya mphesa mmene mungathere kuti mukhute, koma musamaike zina mʼthumba lanu.+

25 Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mnzanu, mungathe kupulula ndi dzanja lanu tirigu amene wacha, koma musamamwete ndi chikwakwa tirigu wa mnzanu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena