Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 19
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Mlandu wa magazi komanso mizinda yothawirako (1-13)

      • Zizindikiro za malire sizinkafunika kusunthidwa (14)

      • Anthu operekera umboni mukhoti (15-21)

        • Pankafunika mboni ziwiri kapena zitatu (15)

Deuteronomo 19:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 7:1; 9:1

Deuteronomo 19:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:14; Yos 20:7, 9

Deuteronomo 19:3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    11/2017, tsa. 14

Deuteronomo 19:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:15; De 4:42

Deuteronomo 19:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:25

Deuteronomo 19:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mtima wake ndi wodzaza ndi ukali.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:12, 19
  • +Yos 20:4, 5

Deuteronomo 19:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18; Eks 23:31; De 11:24
  • +Ge 28:14

Deuteronomo 19:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:22, 23
  • +Yos 20:7, 8

Deuteronomo 19:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 6:16, 17
  • +De 21:6-9

Deuteronomo 19:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Yo 3:15

Deuteronomo 19:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 9:6; Eks 21:12; Nu 35:16; De 27:24

Deuteronomo 19:13

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “diso lanu lisamamumvere.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 24:17, 21; Nu 35:33; 2Sa 21:1

Deuteronomo 19:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 27:17

Deuteronomo 19:15

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “pakamwa pa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:30; De 17:6
  • +Mt 18:16; Yoh 8:17; 2Ak 13:1; 1Ti 5:19

Deuteronomo 19:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:1; 1Mf 21:13; Mko 14:56

Deuteronomo 19:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 17:8, 9

Deuteronomo 19:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:14; 17:4; 2Mb 19:6

Deuteronomo 19:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 19:5
  • +De 21:20, 21; 24:7; 1Ak 5:13

Deuteronomo 19:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:11; 17:13; 1Ti 5:20

Deuteronomo 19:21

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “Diso lanu lisamamve.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 19:13
  • +Eks 21:23-25; Le 24:20; Mt 5:38

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Yandikirani, ptsa. 131-133

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 19:1De 7:1; 9:1
Deut. 19:2Nu 35:14; Yos 20:7, 9
Deut. 19:4Nu 35:15; De 4:42
Deut. 19:5Nu 35:25
Deut. 19:6Nu 35:12, 19
Deut. 19:6Yos 20:4, 5
Deut. 19:8Ge 15:18; Eks 23:31; De 11:24
Deut. 19:8Ge 28:14
Deut. 19:9De 11:22, 23
Deut. 19:9Yos 20:7, 8
Deut. 19:10Miy 6:16, 17
Deut. 19:10De 21:6-9
Deut. 19:111Yo 3:15
Deut. 19:12Ge 9:6; Eks 21:12; Nu 35:16; De 27:24
Deut. 19:13Le 24:17, 21; Nu 35:33; 2Sa 21:1
Deut. 19:14De 27:17
Deut. 19:15Nu 35:30; De 17:6
Deut. 19:15Mt 18:16; Yoh 8:17; 2Ak 13:1; 1Ti 5:19
Deut. 19:16Eks 23:1; 1Mf 21:13; Mko 14:56
Deut. 19:17De 17:8, 9
Deut. 19:18De 13:14; 17:4; 2Mb 19:6
Deut. 19:19Miy 19:5
Deut. 19:19De 21:20, 21; 24:7; 1Ak 5:13
Deut. 19:20De 13:11; 17:13; 1Ti 5:20
Deut. 19:21De 19:13
Deut. 19:21Eks 21:23-25; Le 24:20; Mt 5:38
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 19:1-21

Deuteronomo

19 “Yehova Mulungu wanu akadzawononga mitundu yamʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, inu nʼkuwalandadi dzikolo ndi kukhala mʼmizinda yawo komanso mʼnyumba zawo,+ 2 mudzapatule mizinda itatu pakati pa dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti likhale lanu.+ 3 Mudzagawe mʼzigawo zitatu dziko limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani kuti likhale lanu, ndipo mudzalambule misewu yopita kumizindayo kuti aliyense wopha munthu azithawira kumizinda imeneyo.

4 Ndiye zimene zizichitika ndi munthu amene wapha mnzake nʼkuthawira kumeneko kuti akhale ndi moyo ndi izi: Ngati wapha mnzake mwangozi ndipo sankadana naye,+ 5 mwachitsanzo, munthu akapita ndi mnzake kuthengo kukafuna nkhuni, ndipo wakweza dzanja lake kuti adule mtengo ndi nkhwangwa koma nkhwangwayo yaguluka mumpini wake nʼkumenya mnzakeyo mpaka kumupha, amene wapha mnzakeyo azithawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi kuti akhale ndi moyo.+ 6 Akapanda kutero, chifukwa chakuti wobwezera magazi+ ndi wokwiya kwambiri,* angathamangitse wopha munthuyo nʼkumupeza kenako nʼkumumpha chifukwa chakuti mtunda wopita kumzindawo unali wautali. Koma wopha mnzake mwangoziyo samayenera kufa chifukwa sankadana ndi mnzakeyo.+ 7 Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti, ‘Mupatule mizinda itatu.’

8 Yehova Mulungu wanu akadzawonjezera dziko lanu mogwirizana ndi zimene analumbira kwa makolo anu,+ nʼkukupatsani dziko lonse limene analonjeza makolo anu kuti adzawapatsa,+ 9 (ngati mutatsatira mokhulupirika malamulo onsewa amene ndikukupatsani lero, akuti muzikonda Yehova Mulungu wanu komanso kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse+) mudzawonjezere mizinda inanso itatu pa mizinda imeneyi.+ 10 Mukamachita zimenezi simudzakhetsa magazi a munthu wosalakwa+ mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa ndipo simudzakhala ndi mlandu wa magazi.+

11 Koma ngati munthu amadana ndi mnzake+ ndipo wamubisalira panjira nʼkumuvulaza kwambiri mpaka mnzakeyo kufa, iye nʼkuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, 12 akulu amumzinda wakwawo azimuitanitsa kuchokera kumeneko nʼkumupereka mʼmanja mwa wobwezera magazi ndipo azimupha.+ 13 Musamamumvere* chisoni ndipo muzichotsa mlandu wa magazi a munthu wosalakwa mu Isiraeli+ kuti zinthu zikuyendereni bwino.

14 Mukadzalandira cholowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti likhale lanu musamadzasunthe zizindikiro za malire a mnzanu,+ pamalo amene makolo anu anaika kale malire.

15 Mboni imodzi si yokwanira kutsimikizira kuti munthu wachitadi cholakwa kapena tchimo lililonse.+ Muzitsimikizira nkhaniyo mutamva umboni wochokera kwa* mboni ziwiri kapena zitatu.+ 16 Ngati munthu wakonzera mnzake chiwembu nʼkupereka umboni wonama wakuti waphwanya lamulo,+ 17 anthu awiri amene akukanganawo aziima pamaso pa Yehova, kapena kuti pamaso pa ansembe ndi oweruza amene akuweruza masiku amenewo.+ 18 Oweruzawo azifufuza nkhaniyo mosamala+ ndipo ngati munthu amene anapereka umboniyo wapezeka kuti amanama ndipo waneneza mʼbale wake mlandu wabodza, 19 muzimuchitira zimene amafuna kuti zichitikire mʼbale wakezo,+ ndipo muzichotsa woipayo pakati panu.+ 20 Ena onse adzamva nʼkuchita mantha, ndipo sadzachitanso choipa chilichonse ngati chimenechi pakati panu.+ 21 Musamamve* chisoni.+ Pazikhala moyo kulipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja, phazi kulipira phazi.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena